Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Danieli 6:8-11 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

8. Tsopano, mfumu, mukhazikitse coletsaco, ndi kutsimikiza colembedwaco, kuti cisasinthike monga mwa malamulo a Amedi ndi Aperisi, amene sasinthika.

9. Momwemo mfumu Dariyo anatsimikiza colembedwa ndi coletsaco.

10. Ndipo podziwa Danieli kuti adatsimikiza colembedwaco, analowa m'nyumba mwace, m'cipinda mwace, cimene mazenera ace anatseguka oloza ku Yerusalemu; ndipo anagwadamaondo ace tsiku limodzi katatu, napemphera, nabvomereza pamaso pa Mulungu wace monga umo amacitira kale lonse.

11. Pamenepo anasonkhana anthu awa, napeza Danieli alikupemphera ndi kupembedza pamaso pa Mulungu wace.

Werengani mutu wathunthu Danieli 6