Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Danieli 6:25-28 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

25. Pamenepo mfumu Dariyo analembera kwa anthu, mitundu ya anthu, ndi a manenedwe onse okhala pa dziko lonse lapansi, Mtendere ucurukire inu.

26. Ndilamulira ine kuti m'maiko onse a ufumu wanga anthu anjenjemere, naope pamaso pa Mulungu wa Danieli; pakuti Iye ndiye Mulungu wamoyo wakukhala cikhalire, ndi ufumu wace ngwosaonongeka, ndi kulamulira kwace kudzakhala mpaka cimariziro.

27. Iye apulumutsa, nalanditsa, nacita zizindikilo ndi zozizwa m'mwamba ndi pa dziko lapansi, ndiye amene anapulumutsa Danieli ku mphamvu ya mikango.

28. Momwemo Danieli amene anakuzikabe pokhala Dariyo mfumu, ndi pokhala mfumu Koresi wa ku Perisiya.

Werengani mutu wathunthu Danieli 6