Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Danieli 4:1-10 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

1. Mfumu Nebukadinezara, kwa anthu, mitundu ya anthu, ndi a manenedwe okhala pa dziko lonse lapansi: Mtendere ucurukire inu.

2. Candikomera kuonetsa zizindikilo ndi zozizwa, zimene anandicitira Mulungu Wam'mwambamwamba.

3. Ha! zizindikilo zace nzazikuru, ndi zozizwa zace nza mphamvu, ufumu wace ndiwo ufumu wosatha, ndi kulamulira kwace ku mibadwo mibadwo.

4. Ine Nebukadinezara ndinalimkupumula m'nyumba mwanga, ndi kukhala mwaufulu m'cinyumba canga,

5. Ndinaona loto lakundiopsa, ndi zolingilira za pakama panga, ndi masomphenya a m'mtima mwanga, zinandibvuta ine.

6. Cifukwa cace ndinalamulira kuti adze kwa ine anzeru onse a ku Babulo, kuti andidziwitse kumasulira kwace kwa lotoli.

7. Pamenepo anafika alembi, openda, Akasidi, ndi alauli; ndipo ndinawafotokozera lotoli, koma sanandidziwitsa kumasulira kwace.

8. Koma potsiriza pace analowa pamaso panga Danieli, dzina lace ndiye Belitsazara, monga mwa dzina la mulungu wanga, amenenso muli mzimu wa milungu yoyera m'mtima mwace; ndipo ndinamfotokozera lotoli pamaso pace, ndi kuti,

9. Belitsazara iwe, mkuru wa alembi, popeza ndidziwa kuti mwa iwe muli mzimu wa milungu yoyera, ndi kuti palibe cinsinsi cikusautsa, undifotokozere masomphenya a loto langa ndalotali, ndi kumasulira kwace.

10. Masomphenya a m'mtima mwanga pakama panga ndi awa: Ndinapenya ndi kuona mtengo pakati pa dziko lapansi, msinkhu wace ndi waukuru.

Werengani mutu wathunthu Danieli 4