Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Danieli 3:8-14 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

8. Cifukwa cace anayandikira Akasidi ena nthawi yomweyi, naneneza Ayuda.

9. Anayankha, nati kwa mfumu Nebukadinezara, Mfumu, mukhale ndi moyo cikhalire.

10. Inu mfumu mwalamulira kuti munthu ali yense amene adzamva mau a lipenga, citoliro, zeze, sansi, cisakasa, ngoli, ndi zoyimbitsa ziri zonse, agwadire, nalambire fanolo lagolidi;

11. ndi yense wosagwadira ndi kulambiraadzaponyedwa m'kati mwa ng'anjo yotentha yamoto.

12. Alipo Ayuda amene munawaika ayang'anire nchito ya dera la ku Babulo, Sadrake, Mesake, ndi Abedinego, amuna awa, mfumu, sanasamalira inu, satumikira milungu yanu, kapena kulambira fano lagolidi mudaliimikalo.

13. Pamenepo Nebukadinezara, mumkwiyo ndi m'ukali wace, anawauza abwere nao Sadrake, Mesake, ndi Abedinego. Ndipo anabwera nao amunawa kwa mfumu.

14. Nebukadinezara anayankha, nati kwa iwo, Kodi mutero dala, Sadrake, Mesake, ndi Abedinego, kusatumikira milungu yanga, ndi kusalambira fano lagolidi ndinaliimikalo?

Werengani mutu wathunthu Danieli 3