Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Danieli 3:1-11 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

1. Mfumu Nebukadinezara anapanga fano lagolidi, msinkhu wace mikono makumi asanu ndi limodzi, ndi thunthu lace mikono isanu ndi umodzi; analiimika pa cidikha ca Dura, m'dera la ku Babulo.

2. Ndipo mfumu Nebukadinezara inatumiza kukasonkhanitsa akalonga, akazembe, ndi ziwanga, oweruza, akulu osunga cuma, mandoda, ankhoswe, ndi olamulira onse a madera, abwere kuzurula fanoli adaliimika mfumu Nebukadinezara.

3. Pamenepo akalonga, akazembe, ndi ziwanga, oweruza, akulu osunga cuma, mandoda, ankhoswe, ndi olamulira onse a madera, anasonkhanira kupereka fano adaliimika mfumu Nebukadinezara, naimirira pamaso pa fano adaliimika Nebukadinezara.

4. Ndipo wolalikira anapfuulitsa, kuti, Akulamulirani inu anthu, mitundu ya anthu a manenedwe osiyana,

5. kuti pakumva inu mau a lipenga, citoliro, zeze, sansi, cisakasa, ngoli, ndi zoyimbitsa ziri zonse, mugwadire ndi kulambira fano lagolidi adaliimika mfumu Nebukadinezara;

6. ndipo ali yense wosagwadira ndi kulambira, adzaponyedwa nthawi yomweyo m'kati mwa ng'anjo yotentha yamoto.

7. Potero nthawi yomweyo pakumva anthu onse mau a lipenga, citoliro, zeze, sansi, cisakasa, ndi zoyimbitsa ziri zonse, anthu onse, mitundu ya anthu a manenedwe osiyana, anagwadira, nalambira fano lagolidi adaliimika mfumu Nebukadinezara.

8. Cifukwa cace anayandikira Akasidi ena nthawi yomweyi, naneneza Ayuda.

9. Anayankha, nati kwa mfumu Nebukadinezara, Mfumu, mukhale ndi moyo cikhalire.

10. Inu mfumu mwalamulira kuti munthu ali yense amene adzamva mau a lipenga, citoliro, zeze, sansi, cisakasa, ngoli, ndi zoyimbitsa ziri zonse, agwadire, nalambire fanolo lagolidi;

11. ndi yense wosagwadira ndi kulambiraadzaponyedwa m'kati mwa ng'anjo yotentha yamoto.

Werengani mutu wathunthu Danieli 3