Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Danieli 11:18-27 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

18. Pambuyo pace adzatembenuzira nkhope yace kuzisumbu, nadzalanda zambiri; koma kalonga wina adzaleketsa kunyoza kwace adanyoza nako; inde adzambwezera yekha kunyoza kwace.

19. Pamenepo adzatembenuzira nkhope yace ku malinga a dziko lace lace; koma adzakhumudwa, nadzagwa osapezedwanso.

20. Ndipo m'malo mwace adzauka wina wakupititsa wamsonkho pa ulemerero wa ufumuwo; koma atatha masiku owerengeka adzatyoledwa iye, si mwamkwiyo, kapena kunkhondo ai.

21. Ndi m'malo mwace adzauka munthu woluluka, amene anthu sanampatsa ulemu wa ufumu, koma adzafika kacetecete, nadzalanda ufumu ndi mau osyasyalika.

22. Ndipo mwa mayendedwe ace a cigumula adzakokololedwa pamaso pace, nadzatyoledwa, ngakhale kalonga yemwe wa cipangano.

23. Ndipo atapangana naye adzacita monyenga; pakuti adzakwera, nadzasanduka wamphamvu ndi anthu owerengeka.

24. Adzafika kacetecete ku minda yokometsetsa ya derali, nadzacita cosacita atate ace, kapena makolo ace; adzawawazira zofunkha, ndi zankhondo, ndi cuma, nadzalingiririra malinga ziwembu zace; adzatero nthawi.

25. Nadzautsa mphamvu yace ndi mtima wace ayambane ndi mfumu ya kumwela ndi khamu lalikuru la nkhondo; ndi mfumu ya kumwela ndi khamu lalikuru ndi lamphamvu ndithu; koma sadzaimika, popeza adzamlingiririra ziwembu.

26. Inde iwo akudyako cakudya cace adzamuononga; ndi ankhondo ace adzasefukira, nadzagwaambiri ophedwa.

27. Ndipo mafumu awa onse awiri mitima yao idzakumbuka kucita zoipa, nadzanena bodza ali pa gome limodzi; koma osapindula nalo; pakuti kutha kwace kudzakhala pa nthawi yoikika.

Werengani mutu wathunthu Danieli 11