Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Amosi 1:1-4 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

1. MAU a Amosi, amene anali mwa oweta ng'ombe a ku Tekoa, ndiwo amene anawaona za Israyeli masiku a Uziya mfumu ya Yuda, ndi masiku a Yerobiamu mwana wa Yoasi mfumu ya Israyeli, zitatsala zaka ziwiri cisanafike cibvomezi.

2. Ndipo anati, Yehova adzadzuma ali m'Ziyoni, nadzamveketsa mau ace ali m'Yerusalemu; podyetsa abusa padzacita cisoni, ndi mutu wa Karimeli udzauma.

3. Atero Yehova, Cifukwa ca zolakwa zitatu za Damasiko, kapena zinai, sindidzabweza kulanga kwace; popeza anapuntha Gileadi ndi zopunthira zacitsulo;

4. koma ndidzatumiza moto ku nyumba ya Hazaeli, ndipo udzanyeketsa nyumba zacifumu za Benihadadi.

Werengani mutu wathunthu Amosi 1