Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

2 Samueli 8:10-16 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

10. Toi anatumiza mwana wace Joramu kwa mfumu Davide, kuti akamlankhule iye, ndi kumdalitsa, popeza anamenyana ndi Hadadezeri ndi kumkantha; pakuti pakati pa Hadadezeri ndi Toi panali nkhondo. Ndipo Joramu anabwera ndi zotengera zasiliva, ndi zotengera zagolidi, ndi zotengera zamkuwa.

11. Izi zomwe mfumu Davide anazipatula zikhale za Yehova, pamodzi ndi siliva ndi golidi anapatulako za amitundu onse adawagonjetsa;

12. za Aaramu, za Amoabu, za ana a Amoni, za Afilisti, za Amaleki, ndi zofunkha za Hadadezeri, mwana wa Rehobu mfumu ya ku Zoba.

13. Ndipo Davide anamveketsa dzina lace pamene anabwera uko adakantha Aaramu m'cigwa ca mcere, ndiwo anthu zikwi khumi mphambu zisanu ndi zitatu.

14. Ndipo anaika maboma m'Edomu; m'dziko lonse la Edomu anaika maboma, ndipo Aedomu onse anasanduka anthu a Davide. Ndipo Yehova anasunga Davide kuli konse anamukako.

15. Ndipo Davide anakhala mfumu ya Aisrayeli onse, Davide naweruza ndi cilungamo mirandu ya anthu onse.

16. Ndipo Yoabu mwana wa Zeruya anayang'anira ankhondo, ndi Josafati mwana wa Ahiludi anali wolemba mbiri,

Werengani mutu wathunthu 2 Samueli 8