Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

2 Samueli 6:4-8 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

4. Poturuka nalo tsono pamodzi ndi likasa la Mulungu m'nyumba ya Abinadabu iri pacitunda, Ahio anatsogolera likasalo.

5. Ndipo Davide ndi a nyumba yonse ya Israyeli anasewera pamaso pa Yehova, ndi zoyimbira za mitundu mitundu za mlombwa, ndi azeze, ndi zisakasa ndi malingaka, ndi masece, ndi nsanje.

6. Ndipo pofika iwo ku dwale la Nakoni, Uza anatambasula dzanja lace, nacirikiza likasa la Mulungu; cifukwa ng'ombe zikadapulumuka.

7. Pomwepo mkwiyo wa Yehova udayaka pa Uza, ndipo Mulungu anamkantha pomwepo, cifukwa ca kusalingiriraku; nafa iye pomwepo pa likasa la Mulungu.

8. Ndipo kudaipira Davide, cifukwa Yehova anacita cipasulo ndi Uza; nacha-malowo Cipasulo ca Uza, kufikira lero lino.

Werengani mutu wathunthu 2 Samueli 6