1. Pambuyo pace Davide anamemezanso osankhika onse a m'Israyeli, anthu zikwi makumiatatu.
2. Ndipo Davide ananyamuka, namuka nao anthu onse anali naye, nacokera ku Baale-Yuda natengako likasa la Mulungu, limene amachula nalo Dzinalo Dzina la Yehova wa makamu, wokhala pakati pa Akerubi.