Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

2 Samueli 5:11-16 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

11. Ndipo Hiramu mfumu ya Turo anatumiza mithenga kwa Davide ndi mitengo yamkungudza, ndi amisiri a matabwa, ndi omanga nyumba; iwo nammangira Davide nyumba.

12. Ndipo Davide anazindikira kuti Yehova anamkhazikitsa mfumu ya Israyeli, ndi kuti anakulitsa ufumu wace cifukwa ca anthu ace Israyeli.

13. Ndipo Davide anadzitengera akazi ang'ono ena ndi akazi a ulemu ena a ku Yerusalemu, atafikako kucokera ku Hebroni; ndipo anambadwira Davide ana amuna ndi akazi.

14. Maina a iwo anambadwira m'Yerusalemu ndi awa: Samua, ndi Sobabu, ndi Natani, ndi Solomo,

15. ndi Ibara ndi Elisua, ndi Nefegi ndi Yafiya;

16. ndi Elisama ndi Eliada ndi Elifeleti.

Werengani mutu wathunthu 2 Samueli 5