Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

2 Samueli 4:1-4 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

1. Ndipo pamene Isiboseti mwana wa Sauli, anamva kuti Abineri adakafera ku Hebroni, manja ace anafoka, ndi Aisrayeli onse anabvutika.

2. Ndipo Isiboseti, mwana wa Sauli anali nao amuna awiri, ndiwo atsogoleri a magulu; wina dzina lace Baana, ndi dzina la mnzace ndiye Rekabu, ndiwo ana a Rimoni wa ku Beeroti, wa ana a Benjamini, pakuti Beeroti womwe unawerengedwa wa Benjamini;

3. ndi Abeeroti anathawira ku Gitaimu; kumeneko amakhalira kufikira lero lino.

4. Ndipo Jonatani mwana wa Sauli, anali ndi mwana wamwamuna wopunduka mapazi, Iyeyu anali wa zaka zisanu muja inamveka mbiri ya Sauli ndi Jonatani yocokera ku Jezreeli; ndipo mlezi wace adamnyamula nathawa; ndipo kunali pofulumira kuthawa, iye anagwa nakhala wopunduka. Dzina lace ndiye Mefiboseti.

Werengani mutu wathunthu 2 Samueli 4