Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

2 Samueli 23:6-9 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

6. Koma oipa onse adzakhala ngati minga yoyenera kuitaya,Pakuti siigwiridwa ndi dzanja;

7. Koma wakukhudza iyo adzikonzeratu citsulo ndi luti la mkondo;Ndipo idzatenthedwa konse ndi mota m'malo mwao.

8. Maina a ngwazi Davide anali nazo ndiwo: Josebu-basebete Mtakemoni, mkuru wa akazembe; ameneyu ndiye Adino M-ezni wolimbana ndi mazana atatu ophedwa nthawi imodzi.

9. Ndipo wotsatana naye Eleazeri mwana wa Dodai mwana wa M-akohi, mmodzi wa ngwazi zitatu zokhala ndi Davide pamene iwo anatonza Afilisti osonkhanidwa kunkhondo kumeneko, atacoka Aisrayeli;

Werengani mutu wathunthu 2 Samueli 23