Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

2 Samueli 23:21-30 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

21. ndipo anapha M-aigupto munthu wokongola, M-aigupto anali nao mkondo m'dzanja lace; koma iyeyo anatsikira kwa iye ndi ndodo, nasolola mkondowo m'dzanja la M-aigupto, namupha ndi mkondo wa iye mwini.

22. Izi anacita Benaya mwana wa Yehoyada, natenga dzina mwa ngwazi zitatuzo.

23. Iye ndiye waulemu koposa makumi atatuwo, koma sadafikana ndi atatu oyamba. Ndipo Davide anamuika kuyang'anira olindirira ace.

24. Asaheli mbale wa Yoabu anali wa makumi atatuwo; Elihanani mwana wa Dodo wa ku Betelehemu;

25. Sama Mharodi, Elika Mharodi;

26. Helezi Mpaliti, Ira mwana wa Ikesi Mtekoi.

27. Abiyezeri M-anetori, Mebunai Mhusati;

28. Zalimoni M-ahohi, Maharai Mnefati;

29. Helebi mwana wa Baana Mnetofati, ltai mwana wa Ribai wa ku Gibeya wa ana a Benjamini;

30. Benaya Mpiratoni, Hidai wa ku timitsinje ta Gaasi;

Werengani mutu wathunthu 2 Samueli 23