Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

2 Samueli 22:1-11 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

1. Ndipo Davide analankhula kwa Yehova mau a nyimbo iyi tsikuli Yehova anampulumutsa m'dzanja la adani ace onse, ndi m'dzanja la Sauli.

2. Ndipo anati:-Yehova ndiye thanthwe langa, ndi ngaka yanga, ndi mpulumutsi wanga, wangadi;

3. Mulungu wa thanthwe langa, Iye ndidzamkhulupirira;Cikopa canga, ndi nyanga ya cipulumutso canga, nsanja yanga yaitali, ndi populumukirapo panga;Mpulumutsi wanga, mundipulumutsa kuciwawa.

4. Ndidzaitanakwa Yehovaamene ayenera timtamande;Comweco ndidzapulumutsidwa kwa adani anga.

5. Pakuti mafunde a imfa anandizinga,Mitsinje ya zopanda pace inandiopsa ine.

6. Zingwe za kumanda zinandizingira;Misampha ya imfa inandifikira ine.

7. M'kusauka kwanga ndinaitana kwa Yehova,Inde ndinakuwira kwa Mulungu wanga;Ndipo Iye anamva mau anga ali m'kacisi wace,Ndi kulira kwanga kunafika ku makutuace.

8. Pomwepo dziko linagwedezeka ndi kunthunthumira.Maziko a dziko la kumwamba anasunthikaNagwedezeka, cifukwa iye anakwiya.

9. M'mphuno mwace munaturuka utsi,Ndi moto woturuka m'kamwa mwace unaononga;Makala anayaka nao.

10. Anaweramitsa miyambanso, natsika;Ndipo mdima wandiwe-yani unali pansi pa mapazi ace.

11. Ndipo iye anaberekeka pa Kerubi nauluka;Inde anaoneka pa mapiko a mphepo,

Werengani mutu wathunthu 2 Samueli 22