Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

2 Samueli 20:4-6 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

4. Pamenepo mfumu inati kwa Amasa, Undiitanire anthu a Yuda asonkhane asanapite masiku atatu, nukhale pano iwenso.

5. Comweco Amasa anamuka kukaitana anthu a Yuda asonkhane; koma anacedwa, napitiriza nthawi imene idamuikira.

6. Ndipo Davide anati kwa Abisai, Tsopano Seba mwana wa Bikri adzaticitira coipa coposa cija ca Abisalomu; utenge anyamata a mbuye wako numtsatire, kuti angapeze midzi ya malinga ndi kupulumuka osaonekanso.

Werengani mutu wathunthu 2 Samueli 20