Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

2 Samueli 20:22-26 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

22. Pomwepo mkaziyo anapita kwa anthu onse mwa nzeru yace. Ndipo iwo anadula mutu wa Seba mwana wa Bikri, nauponya kunja kwa Yoabu. Ndipo analiza Gpenga, nabalalika kucoka pamudzipo, munthu yense kumka ku hema wace. Ndipo Yoabu anabwerera kumka ku Yerusalemu kwa mfumu.

23. Ndipo Yoabu anali woyang'anira khamu lonse la Israyeli; ndi Benaya, mwana wa Jehoyada, anayang'anira Akereti ndi Apeleti;

24. ndi Adoramu anayang'anira msonkho; ndi Jehosafati mwana wa Ahiludi anali wolemba mbiri;

25. ndi Seva anali mlembi; ndi Zadoki ndi Abyatara anali ansembe;

26. ndiponso Ira Mjairi anali nduna ya Davide.

Werengani mutu wathunthu 2 Samueli 20