Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

2 Samueli 2:7-9 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

7. Cifukwa cace tsono manja anu alimbike, nimucite camuna; pakuti Sauli mbuye wanu wafa, ndi a nyumba ya Yuda anandidzoza ndikhale mfumu yao.

8. Koma Abineri, mwana wa Neri, kazembe wa khamu la ankhondo a Sauli anatenga Isiboseti mwana wa Sauli, namuolotsa nanka naye ku Mahanaimu;

9. namlonga ufumu wa pa Gileadi ndi Aasuri ndi Jezreeli ndi Efraimu ndi Benjamini ndi Aisrayeli onse.

Werengani mutu wathunthu 2 Samueli 2