Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

2 Samueli 2:27-30 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

27. Yoabu nati, Pali Mulungu, iwe ukadapandakunena, anthu akadabalalika m'mawa osatsata yense mbale wace.

28. Comweco Yoabu anaomba Gpenga, anthu onse naima, naleka kupitikitsa Aisrayeli, osaponyana naonso.

29. Ndipo Abineri ndi anthu ace anacezera usiku wonse kupyola cidikha, naoloka Yordano, napyola Bitroni lonse nafika ku Mahanaimu.

30. Ndipo Yoabu anabwerera pakutsata Abineri. Ndipo pamene anasonkhanitsa pamodzi anthu onse anasowa anthu a Davide khumi ndi asanu ndi anai ndi Asaheli.

Werengani mutu wathunthu 2 Samueli 2