Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

2 Samueli 17:1-7 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

1. Abisalomu, Ndiloleni ndisankhe tsopano anthu zikwi khumi ndi ziwiri, ndipo ndidzanyamuka usiku womwe uno ndi kulondola Davide;

2. ndipo ndidzamgwera ali wolema ndi wofoka, ndi kumuopsa; ndi anthu onse amene ali naye adzathawa; pamenepo ndidzakantha mfumu yokha;

3. ndipo anthu onsewo ndidzabwera nao kwa inu; munthu mumfunayo ali ngati onse obwerera; momwemo anthu onse adzakhala mumtendere.

4. Ndipo mauwa anamuyenerera Abisalomu, ndi akuru onse a Israyeli.

5. Pomwepo Abisalomu anati, Kaitane tsopano Husai M-ariki yemwe, timvenso cimene anene iye.

6. Ndipo pakufika Husai kwa Abisalomu, Abisalomuyo ananena naye, Ahitofeli analankhula mau akuti; ticite kodi monga mwa kunena kwace? ngati iai, unene ndiwe.

7. Ndipo Husai ananena ndi Abisalomu, Uphungu anaupangira lero Ahitofeli suli wabwino.

Werengani mutu wathunthu 2 Samueli 17