Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

2 Samueli 16:12-20 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

12. Kapena Yehova adzayang'anira cosayeneraci alikundicitira ine, ndipo Yehova adzandibwezera cabwino m'malo mwa kunditukwana kwa lero.

13. Comweco Davide ndi anthu ace anapita m'ngra, ndipo Simeyi analambalala paphiri popenyana naye, namuka natukwana, namponya miyala, nawaza pfumbi,

14. Ndipo mfumu ndi anthu onse amene anali naye anafika olema; ndipo iye anadzitsitsimutsa kumeneko.

15. Ndipo Abisalomu, ndi anthu onse amuna a Israyeli, anafika ku Yerusalemu, ndi Ahitofeli pamodzi naye.

16. Ndipo kunali pakudza kwa Abisalomu Husai M-ariki, bwenzi la Davide, Husai ananena ndi Abisalomu, Mfumu ikhale ndi moyo, Mfumu ikhale ndi moyo.

17. Ndipo Abisalomu ananena ndi Husai, Kodi cimeneci ndi cifundo cako ca pa bwenzi lako? unalekeranji kupita ndi bwenzi lako?

18. Husai nanena ndi Abisalomu, lai; koma amene Yehova anasankha ndi anthu awa, ndi anthu onse a Israyeli, ine ndiri wace, ndipo ndidzakhala naye iyeyu.

19. Ndiponso ndidzatumikira yani? si pamaso pa mwana wace nanga? monga ndinatumikira pamaso pa atate wanu, momwemo ndidzakhala pamaso panu,

20. Pomwepo Abisalomu ananena ndi Ahitofeli, Upangire cimene ukuti rikacite.

Werengani mutu wathunthu 2 Samueli 16