Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

2 Samueli 15:12-14 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

12. Ndipo Abisalomu anaitana Ahitofeli Mgiloni, mphungu wa Davide, ku mudzi wace ndiwo Gilo, pamene iye analikupereka nsembe. Ndipo ciwembuco cinali colimba; pakuti anthu anacurukacurukabe kwa Abisalomu.

13. Ndipo mthenga unafika kwa Davide nuti, Mitima ya anthu a Israyeli itsata Abisalomu.

14. Ndipo Davide ananena nao anyamata ace onse akukhala naye ku Yerusalemu, Nyamukani tithawe, tikapanda kuthawa palibe mmodzi wa ife adzapulumuka Abisalomu; fulumirani kucoka, angatipeze msanga ndi kutigwetsera zoipa ndi kukantha mudzi ndi lupanga lakuthwa.

Werengani mutu wathunthu 2 Samueli 15