Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

2 Samueli 14:31-33 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

31. Pamenepo Yoabu ananyamuka nafika kwa Abisalomu ku nyumba yace, nanena naye, Cifukwa ninji anyamata anu anatentha za m'munda mwanga;

32. Abisalomu nayankha Yoabu, Ona, ndinatumiza kwa iwe kuti, Bwera kuno kuti ndikutume kwa mfumu kukanena, Ine ndinabwereranji kucokera ku Gesuri? mwenzi nditakhala komweko; cifukwa cace tsono mundilole kuona nkhope ya mfumu; ndipo ngati mulinso mphulupulu mwa ine andiphe ndithu.

33. Comweco Yoabu anadza kwa mfumu namuuza; ndipo pamene iye adaitana Abisalomu, iye anadza kwa mfumu naweramira nkhope yace pansi pamaso pa mfumu; ndipo mfumu inampsompsona Abisalomu.

Werengani mutu wathunthu 2 Samueli 14