Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

2 Samueli 14:21-25 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

21. Ndipo mfumuyo inanena ndi Yoabu, Taonatu, ndacita cinthu ici; cifukwa cace, pita nubwere nayenso mnyamatayo Abisalomu.

22. Ndipo Yoabu anagwa nkhope yace pansi, namlambira, nadalitsa mfumuyo; nati Yoabu, Lero mnyamata wanu ndadziwa kuti munandikomera mtima, mbuye wanga mfumu, popeza mfumu yacita copempha mnyamata wace.

23. Comweco Yoabu ananyamuka namka ku Gesuri, nabwera naye Abisalomu ku Yerusalemu.

24. Ndipo mfumu inati, Apambukire ku nyumba yaiye yekha, koma asaone nkhope yanga. Comweco Abisalomu anapambukira ku nyumba ya iye yekha, wosaona nkhope ya mfumu.

25. Ndipo m'lsrayeli monse munalibe wina anthu anamtama kwambiri cifukwa ca kukongola kwace monga Abisalomu; kuyambira ku mapazi kufikira pakati pa mutu wace mwa iye munalibe cirema.

Werengani mutu wathunthu 2 Samueli 14