23. Ndipo zitapita zaka ziwiri zathunthu, kunali kuti Abisalomu anali: nao osenga nkhosa zace ku Baalahazore pafupi pa Efraimu; ndipo Abisalomu anaitana ana amuna onse a mfumu.
24. Abisalomu nafika kwa mfumu nati, Onani, ine mnyamata, wanu ndiri nao osenga nkhosa; inu mfumu ndi anyamata anu mupite nane mnyamata wanu.
25. Ndipo mfumu inati kwa Abisalomu, lai mwana wanga, tisapite tonse, kuti tingakucurukire. Ndipo iye anaiumirira koma inakana kupita; koma inamdalitsa.
26. Pomwepo Abisalomu anati, Ngati nkutero, mulole mbale wanga Amnoni apite nafe. Ndipo mfumu inanena naye, iye apitirenji nawe?