Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

2 Samueli 13:14-17 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

14. Koma iye sadafuna kumvera mau ace, ndipo popeza anali wamphamvu ndi iye, anamkangamiza, nagona naye.

15. Atatero Amnoni anadana naye ndi cidani cacikuru kopambana; pakuti cidani cimene anamuda naco, cinali cacikuru koposa cikondi adamkonda naco. Ndipo Amnoni ananena naye, Nyamuka, coka.

16. Koma iye ananena naye, Usamatero, pakuti coipa ici cakuti ulikundipitikitsa ncacikuru coposa cina cija unandicitira ine. Kama anakana kumvera.

17. Pomwepo anaitana mnyamata wace amene anamtumikira, nati, Turutsa mkazi uyu kwa ine, nupiringidze citseko atapita iye.

Werengani mutu wathunthu 2 Samueli 13