Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

2 Samueli 11:21-27 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

21. Ndani anakantha Abimeleki mwana wa Jerubeseti? Sadamponyera kodi mphero mkazi wa palinga nafa iye ku Tebezi? Munasendera bwanji pafupi potere pa lingalo? Tsono udzanena, Mnyamata wanu Uriya Mhiti, iyenso adafa,

22. Comweco mthengawo unamuka, nufika, nudziwitsa Davide zonse Yoabu anamtumiza.

23. Ndipo mthengawo unati kwa Davide, Anthuwo anatilaka naturukira kwa ife kumundako, koma tinawa gwera kufikira polowera kucipata,

24. Ndipo akuponyawo amene anali palinga anaponya anyamata anu; ndipo anyamata ena a mfumu anafa, ndi mnyamata wanu Uriya Mhiti, iyenso anafa.

25. Pomwepo Davide ananena ndi mthengawo, Udzatero kwa Yoabu, Cisakuipire ici, lupanga limaononga ina ndi mnzace. Onjeza kulimbitsa nkhondo yako pamudzipo, nuupasule; numlimbikitse motere.

26. Ndipo pamene mkazi wa Uriya anamva kuti Uriya mwamuna wace adamwalira, iye analira maliro a mwamuna wace.

27. Ndipo pakuturuka malirowo, Davide anatumiza munthu namtenga afike kwao ku nyumba yace; ndipo iyeyo anakhala mkazi wace nambalira mwana wamwamuna. Koma Yehova anaipidwa ndi cinthu cimene Davide adacita.

Werengani mutu wathunthu 2 Samueli 11