Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

2 Mbiri 9:16-27 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

16. Napanganso malihawo mazana atatu a golidi wonsansantha, cikopa cimodzi cinathera masekeli mazana atatu a golidi; ndipo mfumu inazilonga m'nyumba yochedwa Nkhalango ya Lebano.

17. Mfumu inapanganso mpando wacifumu waukuru wa minyanga, naukuta ndi golidi woona.

18. Ndi mpando wacifumuwo unali nao makwerero asanu ndi limodzi, ndi copondapo mapazi cagolidi, omangika ku mpandowo; ndi ku mbali zonse ziwiri za pokhalirapo kunali manja; ndi mikango iwiri inaimirira m'mbali mwa manjawo.

19. Ndi mikango khumi ndi iwiri Inaimirirapo, mbali yina ndi yina, pa makwerero asanu ndi limodzi; sanapangidwa wotere m'ufumu uli wonse.

20. Ndipo zikho zomwera zonse za Solomo zinali zagolidi, ndi zipangizo zonse za nyumba yochedwa Nkhalango ya Lebano zinali za golidi woona; siliva sanayesedwa kanthu m'masiku a Solomo.

21. Pakuti zombo za mfumu zinayenda ku Tarisi ndi anyamata a Huramu; zombo za ku Tarisi zinadza kamodzi zitapita zaka zitatu, ndi kubwera nazo golidi, ndi siliva, minyanga, ndi apusi, ndi mbalame za zitsukwa zazitali za mawanga mawanga.

22. Mamwemo mfumu Solomo inaposa mafumu onse a pa dziko lapansi, kunena za cuma ndi nzeru.

23. Ndipo mafumu onse a pa dziko lapansi anafuna nkhope ya Solomo, kudzamva nzeru zace Mulungu adazilonga m'mtima mwace.

24. Nabwera nao munthu yense mtulo wace, zipangizo zasiliva, ndi zipangizo zagolidi, zobvala, ndi zobvala za nkhondo, ndi zonunkhira, akavalo, ndi nyuru; momwemo caka ndi caka.

25. Ndipo Solomo anali nazo zipinda zikwi zinai za akavalo ndi magareta, ndi apakavalo zikwi khumi ndi ziwiri; nawaika m'toidzi ya magareta, ndi m'Yerusalemu kwa mfumu.

26. Ndipo analamulira mafumu onse kuyambira ku Firate kufikira ku dziko la Afilisti, ndi ku malire a ku Aigupto.

27. Ndipo mfumu inacurukitsa siliva m'Yerusalemu ngati miyala; ndi mikungudza anailinganiza ndi mikuyu iri kumadambo kucuruka kwace.

Werengani mutu wathunthu 2 Mbiri 9