Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

2 Mbiri 5:1-8 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

1. Momwemo zidatha nchito zonse Solomo adazicitira nyumba ya Yehova. Ndipo Solomo anabwera nazo zopatulika zija za atate wace Davide; naziika siliva, ndi golidi, ndi zipangizo zonse m'cuma ca nyumba ya Mulungu.Kuperekedwa kwa Kacisi.

2. Pamenepo Solomo anasonkhanitsira akulu akulu a Israyeli, ndi akuru onse a mafuko, ndi akalonga a nyumba za makolo a ana a Israyeli, ku Yerusalemu, kukatenga likasa la cipangano ca Yehova ku mudzi wa Davide ndiwo Zioni.

3. Ndipo amuna onse a Israyeli anasonkhana kwa mfumu kumadyerero anacitikawo, m'mwezi wacisanu ndi ciwiri.

4. Nadza akulu akulu onse a Israyeli, nanyamula likasalo Alevi.

5. Ndipo anakwera nalo likasa, ndi cihema cokomanako, ndi zipangizo zonse zopatulika zinali m'cihemamo; izizo ansembe Alevi anakwera nazo.

6. Ndi mfumu Solomo ndi khamu lonse la Israyeli losonkhana kwa iye anali kulikasa, naphera nsembe, nkhosa ndi ng'ombe zosawerengeka kucuruka kwace.

7. Ndipo ansembe analowa nalo likasa la cipangano la Yehova kumalo kwace m'moneneramo mwa kacisi, m'malo opatulikitsa, pansi pa mapiko a akerubi.

8. Pakuti akerubi anafunyulula mapiko ao pa malo a likasa, ndi akerubi anaphimba likasa ndi mphiko zace pamwamba pace.

Werengani mutu wathunthu 2 Mbiri 5