Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

2 Mbiri 32:17-20 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

17. Analemberanso akalata a kunyoza Yehova Mulungu wa Israyeli, ndi kunena motsutsana ndi Iye, ndi kuti, Monga milungu ya mitundu ya anthu a m'maiko, imene siinalanditsa anthu ao m'dzanja langa, momwemo Mulungu wa Hezekiya sadzalanditsa anthu ace m'dzanja mwanga.

18. Ndipo anapfuula ndi mau akuru m'cinenedwe ca Ayuda kwa anthu a m'Yerusalemu okhala palinga, kuwaopsa ndi kuwabvuta, kuti alande mudziwu.

19. Nanenera Mulungu wa Yerusalemu, monga umo amanenera milungu ya mitundu ya anthu a pa dziko lapansi, ndiyo nchito ya manja a anthu.

20. Ndipo Hezekiya mfumu, ndi Yesaya mneneri mwana wa Amozi, anapemphera pa ici, napfuulira Kumwamba.

Werengani mutu wathunthu 2 Mbiri 32