Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

2 Mbiri 29:32-36 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

32. Ndi kuwerenga kwace kwa nsembe zopsereza unabwera nazo msonkhanowo ndiko ng'ombe makumi asanu ndi awiri, nkhosa zamphongo zana limodzi, ndi ana a nkhosa mazana awiri; zonsezi nza nsembe yopsereza ya Yehova.

33. Ndi zinthu, zopatulika zinafikira ng'ombe mazana asanu ndi limodzi, ndi nkhosa zikwi zitatu.

34. Koma ansembe anaperewera, osakhoza kusenda nsembe zonse zopsereza; m'mwemo abale ao Alevi anawathandiza, mpaka idatha nchitoyi, mpaka ansembe adadzipatula; pakuti Alevi anaposa ansembe m'kuongoka mtima kwao kudzipatula.

35. Ndiponso zidacuruka nsembe zopsereza, pamodzi ndi mafuta a nsembe zamtendere, ndi nsembe zothira za nsembe yopsereza iri yonse. Momwemo utumiki wa nyumba ya Yehova unalongosoka.

36. Nakondwera Hezekiya ndi anthu onse pa ici Mulungu adakonzeratu; pakuti cinthuci cidacitika modzidzimutsa.

Werengani mutu wathunthu 2 Mbiri 29