Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

2 Mbiri 22:7-10 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

7. Kuonongeka kwa Ahaziya tsono nkwa Mulungu, kuti amuke kwa Yehocamu; pakuti atafika anaturukira pamodzi ndi Yehoramu kukayambana ndi Yehu mwana wa Nimsi, amene Yehova anamdzoza alikhe nyumba ya Ahabu.

8. Ndipo kunali, pakulanga Yehu nyumba ya Ahabu, anapeza akalonga a Israyeli, ndi ana a abale a Ahaziya, akutumikira Ahaziya, nawapha.

9. Atatero, anafunafuna Ahaziya, namgwira alikubisala m'Samariya, nabwera naye kwa Yehu, namupha; ndipo anamuika; pakuti anati, Ndiye mwana wa Yehosafati, wofuna Yehova ndi mtima wace wonse. Ndipo panalibe wina wa nyumba ya Ahaziya wa mphamvu yakusunga ufumuwo.

10. Pamene Ataliya anaona kuti mwana wace adafa, anauka, naononga mbeu yonse yacifumu ya nyumba ya Yuda.

Werengani mutu wathunthu 2 Mbiri 22