Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

2 Mbiri 11:17-20 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

17. Momwemo analimbikitsa ufumu wa Yuda, nalimbikitsa Rehabiamu, mwana wa Solomo zaka zitatu; pakuti anayenda m'njira ya Davide ndi Solomo zaka zitatu.

18. Ndipo Rehabiamu anadzitengera mkazi Mahalati, mwana wamkazi wa Yerimoti mwana wa Davide, ndi wa Abihaili mwana wamkazi wa Eliabu mwana wa Jese;

19. ndipo anambalira ana, Yeusi, ndi Semariya, ndi Zahamu.

20. Ndi pambuyo pace anatenga Maaka mwana wamkazi wa Abisalomu; ndipo anambalira Abiya, ndi Atai, ndi Ziza, ndi Selomiti.

Werengani mutu wathunthu 2 Mbiri 11