Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

2 Mafumu 9:10-14 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

10. Ndipo agaru adzamudya Yezebeli pa dera la Yezreeli, wopanda wina wakumuika. Pamenepo anatsegula pakhomo, nathawa.

11. Ndipo Yehu anaturukira kwa anyamata a mbuye wace, nanena naye wina, Mtendere kodi? anakudzera cifukwa ninji wamisala uyu? Nanena nao, Mumdziwa munthuyo ndi makambidwe ace.

12. Nati iwo, Kunama uku; utifotokozere tsono. Nati iye, Anati kwa ine cakuti cakuti; ndi kuti, Atero Yehova, Ndakudzoza mfumu pa Israyeli.

13. Nafulumira iwo, nagwira yense copfunda cace, naciyala pokhala iye paciunda, naomba lipenga, nati, Yehu ndiye mfumu.

14. Motero Yehu mwana wa Yehosafati mwana wa Nimsi anapandukira Yoramu. Tsono Yoramu atalindira ku Ramoti Gileadi, iye ndi Aisrayeli onse, cifukwa ca Hazaeli mfumu ya Aramu;

Werengani mutu wathunthu 2 Mafumu 9