Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

2 Mafumu 7:1-3 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

1. Ndipo Elisa anati, Mverani mau; a Yehova; atero Yehova, Mawa dzuwa lino adzagula muyeso wa ufa ndi sekeli, adzagulanso miyeso iwiri ya barele ndi sekeli, pa cipata ca Samariya.

2. Pamenepo kazembe amene mfumu adafotsamira pa dzanja lace anamyankha munthu wa Mulungu, nati, Taonani, Yehova angacite mazenera m'mwamba cidzacitika ici kodi? Nati iye, Taona, udzaciona ndi maso ako, koma iwe sudzadyako ai.

3. Koma polowera pa cipata panali amuna anai akhate, nanenana wma ndi mnzace, Tikhaliranji kuno mpaka kufa?

Werengani mutu wathunthu 2 Mafumu 7