Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

2 Mafumu 6:5-9 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

5. Ndipo wina analinkudula mtengo nkhwangwa inagwa m'madzi; ndipo anapfuula, nati, Kalanga ine mbuyanga! popeza ojobwereka.

6. Nati munthu wa Mulungu, Yagwera pati? Namuonetsapo yagwera. Pamenepo anadula kamtengo, nakaponya pomwepo, nayandamitsa nkhwangwayo.

7. Nati, Katole. Natambasula dzanja lace, naitenga.

8. Ndipo mfumu ya Aramu inalinkucita nkhondo ndi Israyeli, nipangana ndi anyamata ace, kuti, Misasa yanga idzakhala pakuti pakuti.

9. Ndipo munthu wa Mulunguyo anatuma mau kwa mfumu ya Israyeli, ndi kuti, Mucenjere musapite pakuti, popeza Aaramu alikutsikira uko.

Werengani mutu wathunthu 2 Mafumu 6