Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

2 Mafumu 4:8-17 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

8. Ndipo linafika tsiku lakuti Elisa anapitirira kumka ku Sunemu, kumeneko kunali mkazi womveka; ameneyo anamuumiriza adye mkate. Potero pomapitirako iyeyu, adafowapa, mbukirako kukadya mkate.

9. Ndipo mkaziyo anati kwa mwamuna wace, Taona, tsopano ndidziwa kuti munthu uyu wakupitira pathu pano cipitire ndiye munthu woyera wa Mulungu.

10. Timmangire kacipinda kosanja, timuikirenso komweko kama, ndi gome, ndi mpando, ndi coikapo nyali; ndipo kudzatero kuti akatidzera alowe m'mwemo.

11. Ndipo linadza tsiku lakuti anafikako, nalowa m'cipinda cosanja, nagona komweko.

12. Nati kwa Gehazi mnyamata wace, Itana Msunemu uja. Namuitana, naima mkaziyo pamaso pace.

13. Ndipo anati kwa iye, Ufunse mkaziyu tsopano, kuti, Taona watisungira ndi kusamalira uku konse; nanga tikucitire iwe ciani? Kodi tikunenere kwa mfumu, kapena kwa kazembe wa nkhondo? Koma anati, Ndikhala ine pakati pa anthu a mtundu wanga.

14. Pamenepo anati, Nanga timcitire iye ciani? Nati Gehazi, Zedi alibe mwana, ndi mwamuna wace wakalamba.

15. Nati, Kamuitane. Namuitana, naima pakhomo mkaziyo.

16. Ndipo anati, Nyengo yino caka cikudzaci udzafukata mwana wamwamuna. Koma anati, lai, mbuyanga, munthu wa Mulungu, musanamiza mdzakazi wanu.

17. Ndipo mkaziyo anaima, naona mwana wamwamuna nyengo yomweyo caka cimene cija Elisa adanena naye.

Werengani mutu wathunthu 2 Mafumu 4