Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

2 Mafumu 4:1-10 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

1. Ndipo wina wa akazi a ana a aneneri anapfuula kwa Elisa, ndi kuti, Mnyamata wanu, mwamuna wanga wafa; mudziwa kuti mnyamata wanu anaopa Yehova; ndipo wafika wamangawa kunditengera ana anga awiri akhale akapolo ace.

2. Ndipo Elisa anati kwa iye, Ndikucitire ciani? undiuze m'nyumba mwako muli ciani? Nati, Mdzakazi wanu alibe kanthu m'nyumba, koma mtsuko wa mafuta.

3. Pamenepo anati, Kabwereke zotengera kwina kwa anansi ako onse, zotengera zopanda kanthu, zisakhale pang'ono.

4. Nulowe, uudzitsekere wekha ndi ana ako amuna ndi kutsanulira m'zotengera zonsezi, nuike padera zodzalazo.

5. Pamenepo anamcokera, nadzitsekera yekha ndi ana ace amuna; iwo namtengera zotengerazo, iye namatsanulira.

6. Ndipo kunali, zitadzala zotengera, anati kwa mwana wace, Nditengere cotengera cina, Nanena naye, Palibe cotengera cina. Ndipo mafuta analeka.

7. Pamenepo anadza, namfotokozera munthu wa Mulungu. Nati iye, Kagulitse mafuta, ukabwezere mangawa ako, ndi zotsalapo zikusunge iwe ndi ana ako.

8. Ndipo linafika tsiku lakuti Elisa anapitirira kumka ku Sunemu, kumeneko kunali mkazi womveka; ameneyo anamuumiriza adye mkate. Potero pomapitirako iyeyu, adafowapa, mbukirako kukadya mkate.

9. Ndipo mkaziyo anati kwa mwamuna wace, Taona, tsopano ndidziwa kuti munthu uyu wakupitira pathu pano cipitire ndiye munthu woyera wa Mulungu.

10. Timmangire kacipinda kosanja, timuikirenso komweko kama, ndi gome, ndi mpando, ndi coikapo nyali; ndipo kudzatero kuti akatidzera alowe m'mwemo.

Werengani mutu wathunthu 2 Mafumu 4