Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

2 Mafumu 3:6-10 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

6. Ndipo mfumu Yehoramu anaturuka m'Samariya nthawi yomweyo, namemeza Aisrayeli onse.

7. Nakatumiza mau kwa Yehosafati mfumu ya Yuda, ndi kuti, Mfumu ya Moabu wapandukana ndi ine; kodi udzamuka nane kukathira nkhondo pa Moabu? Nati, Ndidzakwera: ine ndikhala ngati iwe, anthu anga ngati anthu ako, akavalo anga ngati akavalo ako.

8. Ndipo anati, Tikwerere njira yiti? Nati iye, Njira ya ku cipululu ca Edomu.

9. Namuka mfu mu ya Israyeli, ndi mfumu ya Yuda, ndi mfumu ya Edomu, nazungulira njira ya masiku asanu ndi awiri; ndipo panalibe madzi kuti ankhondo amwe, kapena nyama zakuwatsata.

10. Ndipo mfumu ya Israyeli inati, Kalanga ife! pakuti Yehova waitana mafumu ife atatu kutipereka m'dzanja la Moabu.

Werengani mutu wathunthu 2 Mafumu 3