Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

2 Mafumu 23:27-31 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

27. Nati Yehova, Ndidzacotsa Yudanso pamaso panga, monga umo ndinacotsera Israyeli; ndipo ndidzataya mudzi uwu ndidausankha, ndiwo Yerusalemu, ndi nyumba ndidainena, Dzina langa lidzakhala komweko.

28. Macitidwe ena tsono a Yosiya, ndi zonse anazicita, sizilembedwa kodi m'buku la macitidwe a mafumu a Yuda?

29. Masiku ace Farao-Neko mfumu ya Aigupto anakwerera mfumu ya Asuri ku mtsinje wa Firate; Ddipo mfumu Yosiya anaturuka kuponyana naye, koma anapha Yosiya ku Megido, atamuona.

30. Ndipo anyamata ace anamtengera wakufa m'gareta, nabwera naye ku Yerusalemu kucokera ku Megido, namuika m'manda ace ace. Ndipo anthu a m'dziko anatenga Yoahazi mwana wa Yosiya, namdzoza, namlonga ufumu m'malo mwa atate wace.Yoahazi, Yoyakimu ndi Yoyakini mafumu oipa a Yuda.

31. Yoahazi anali wa zaka makumi awiri mphambu zitatu polowa ufumu wace, nakhala mfumu miyezi itatu m'Yerusalemu ndi dzina la mace ndiye Hamutali mwana wa Yeremiya wa ku Libina.

Werengani mutu wathunthu 2 Mafumu 23