Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

2 Mafumu 23:24-28 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

24. Ndiponso obwebweta, ndi openda, ndi aterafi, ndi mafano, ndi zonyansa zonse zidaoneka m'dziko la Yuda ndi m'Yerusalemu, Yosiya anazicotsa; kuti alimbitse mau a cilamulo olembedwa m'buku adalipeza Hilikiya wansembe m'nyumba ya Yehova.

25. Ndipo asanabadwe iye panalibe mfumu wolingana naye, imene inatembenukira kwa Yehova ndi mtima wace wonse, ndi moyo wace wonse, ndi mphamvu yace yonse, monga mwa cilamulo conse ca Mose; atafa iyeyu sanaukanso wina wolingana naye.

26. Koma Yehova sanakululuka mkwiyo wace waukuru waukali umene adapsa mtima nao pa Yuda, cifukwa ca zoputa zonse Manase adaputa nazo mkwiyo wace.

27. Nati Yehova, Ndidzacotsa Yudanso pamaso panga, monga umo ndinacotsera Israyeli; ndipo ndidzataya mudzi uwu ndidausankha, ndiwo Yerusalemu, ndi nyumba ndidainena, Dzina langa lidzakhala komweko.

28. Macitidwe ena tsono a Yosiya, ndi zonse anazicita, sizilembedwa kodi m'buku la macitidwe a mafumu a Yuda?

Werengani mutu wathunthu 2 Mafumu 23