Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

2 Mafumu 23:16-21 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

16. Ndipo potembenuka Yosiya anaona manda okhalako kuphiri, natumiza anthu naturutsa mafupa kumanda, nawatentha pa guwa la nsembe, kuliipitsa, monga mwa mau a Yehova anawalalikira munthu wa Mulungu wolalikira izi.

17. Anatinso, Cizindikilo ici ndiciona nciani? Namuuza anthu a m'mudziwo, Ndico manda a munthu wa Mulungu anafuma ku Yuda, nalalikira izi mwazicitira guwa la nsembe la ku Beteli.

18. Nati iye, Mlekeni, munthu asakhudze mafupa ace. Naleka iwo mafupa ace akhale pamodzi ndi mafupa a mneneri uja anaturuka m'Samariya.

19. Ndi nyumba zonse zoo mwe za ku misanje yokhala m'midzi ya Samariya, adazimanga mafumu a Israyeli kuutsa nazo mkwiyo wa Yehova, Yosiya anazicotsa, nazicitira monga mwa nchito zonse adazicita ku Beteli.

20. Ndipo anapha ansembe onse a misanje okhalako pa maguwa a nsembe, natentha-mafupa a anthu pamenepo, nabwerera kumka ku Yerusalemu.

21. Ndipo mfumu inalamulira anthu onse, kuti, Mcitireni Yehova Mulungu wanu Paskha, monga mulembedwa m'buku ili la cipangano,

Werengani mutu wathunthu 2 Mafumu 23