Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

2 Mafumu 22:10-16 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

10. Ndipo Safani mlembiyo anafotokozera mfumu, ndi kuti, Hilikiya wansembe wandipatsa buku. Nawerengamo Safani pamaso pa mfumu.

11. Ndipo kunali, atamva mfumu mau a m'buku la cilamulo, inang'amba zobvala zace.

12. Ndipo mfumu inalamulira Hilikiya wansembe, ndi Ahikamu mwana wa Safani, ndi Alabori mwana wa Mikaya, ndi Safani mlembi, ndi Asaya mnyamata wa mfumu, ndi kuti,

13. Mukani, funsirani ine, ndi anthu, ndi Yuda yense, kwa Yehova za mau a buku ili adalipeza; pakuti mkwiyo wa Yehova wotiyakira ife ndi waukuru; popeza atate athu sanamvera mau a buku ili, kucita monga mwa zonse zotilemberamo.

14. Namuka Hilikiya wansembe, ndi Ahikamu, ndi Akibori, ndi Safani, ndi Asaya, kwa Hulida mneneri wamkazi, ndiye mkazi wa Salumu mwana wa Tlkiva, mwana wa Harasi, wosunga zobvala za mfumu; analikukhala iye m'Yerusalemu m'dera laciwiri, nalankhula naye.

15. Ndipo Hulida ananena nao, Atero Yehova Mulungu wa Israyeli, Muuze munthuyo anakutumizani kwa ine,

16. Atero Yehova, Ta, onani, nditengera maloano coipa, ndi iwo okhalamo, cokwaniritsa mau onse a m'buku adaliwerenga mfumu ya Yuda;

Werengani mutu wathunthu 2 Mafumu 22