Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

2 Mafumu 20:1-4 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

1. Masiku ajawo Hezekiya anadwala, nafuna kufa. Namdzera Yesaya mneneri mwana wa Amozi, nanena naye, Atero Yehova, Siyira banja lako; pakuti udzafa, sudzakhala ndi moyo.

2. Pamenepo anatembenuzira nkhope yace kukhoma, napemphera kwa Yehova, ndi kuti,

3. Mukumbukile Yehova kuti ndinayendabe pamaso panu m'coonadi, ndi mtima wangwiro, ndi kucita zokoma m'kuona kwanu. Nalira Hezekiya kulira kwakukuru.

4. Ndipo kunali, asanaturukire Yesaya m'kati mwa mudzi, anamdzera mau a Yehova, ndi kuti,

Werengani mutu wathunthu 2 Mafumu 20