Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

2 Mafumu 2:18-22 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

18. Nabwerera kwa iye ali cikhalire ku Yeriko, ndipo anati kwa iwo, Kodi sindinanena nanu, Musamuka?

19. Ndipo amuna a kumudzi anati kwa Elisa, Taonani, pamudzi pano mpabwino, monga umo aonera mbuye wanga; koma madzi ndi oipa, ndi nthaka siibalitsa.

20. Pamenepo anati, Nditengereni cotengera catsopano, muikemo mcere. Ndipo anabwera naco kwa iye.

21. Ndipo anaturuka kumka ku magwero a madzi, nathiramo mcere, nati, Atero Yehova, Ndaciritsa madzi awa, sikudzafumirakonso imfa, kapena kusabalitsa.

22. Cotero madzi anaciritsidwa mpaka lero lino, monga mwa mau a Elisa ananenawo.

Werengani mutu wathunthu 2 Mafumu 2