Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

2 Mafumu 2:1-3 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

1. Ndipo kunali, pamene Yehova adati akweze Eliya kumwamba ndi kabvumvulu, Eliya anacokera ku Giligala pamodzi ndi Elisa.

2. Ndipo Eliya anati kwa Elisa, Ukhale pompano pakuti Yehova wandituma ndimke ku Beteli. Nati Elisa, Pali Mulungu, pali inu, sindikusiyani. Motero anatsikira iwo ku Beteli.

3. Ndipo ana a aneneri okhala ku Beteli anaturukira Elisa, nanena naye, Kodi udziwa kuti Yehova akucotsera lero mbuye wako, mtsogoleri wako? Nati, lode ndidziwa, khalani muli cete.

Werengani mutu wathunthu 2 Mafumu 2