Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

2 Mafumu 19:27-37 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

27. Koma ndidziwa kukhala pansi kwako, ndi kuturuka kwako, ndi kulowa kwako, ndi kundizazira kwako.

28. Cifukwa ca kundizazira kwako, ndi popeza kudzikuza kwako kwandifikira m'makutu mwanga, ndidzakukowa ndi ngowe yanga m'mphuno mwako, ndi cam'kamwa canga m'milomo mwako; ndipo ndidzakubwezera pa njira unadzerayi.

29. Ndi ici ndi cizindikilo cako: caka cino mudzadya za mphulumukwa, ndi caka ca mawa za mankhokwe, ndi caka camkuca muzibzala ndi kukolola, muzioka minda yampesa ndi kudya zipatso zace.

30. Ndipo opulumuka a nyumba ya Yuda otsalawo adzaphukanso mizu, ndi kupatsa zipatso pamwamba.

31. Pakuti ku Yerusalemu kudzaturuka otsala, ndi akupulumukawo ku phiri la Ziyoni; cangu ca Yehova cidzacita ici.

32. Cifukwa cace atero Yehova za mfumu ya Asuri, iye sadzalowa m'mudzi muno, kapena kuponyamo mubvi, kapena kufikako ndi cikopa, kapena kuundira mtumbira.

33. Adzabwerera njira yomweyo anadzera, ndipo sadzalowa m'mudzi muno, ati Yehova.

34. Pakuti ndidzacinjiriza mudzi uno kuupulumutsa, cifukwa ca Ine mwini, ndi cifukwa ca Davide mtumiki wanga.

35. Ndipo kunali, usiku womwewo mthenga wa Yehova anaturuka, nakantha m'misasa ya Aasuri zikwi zana limodzi mphambu makumi asanu ndi atatu kudza zisanu, ndipo pouka anthu mamawa, taonani, onsewo ndi mitembo.

36. Nacoka Sanakeribu mfumu ya Asuri, namuka, nabwerera, nakhala ku Nineve.

37. Ndipokunali popembedza iye m'nyumba ya Nisiroki mulungu wace, Adrameleki ndi Sarezere anamkantha ndi lupanga; napulumukira ku dziko la Ararati. Ndipo Esarihadoni mwana wace anakhala mfumu m'malo mwace.

Werengani mutu wathunthu 2 Mafumu 19