Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

2 Mafumu 19:14-18 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

14. Ndipo Hezekiya analandira kalatayo ku dzanja la mithenga, namwerenga, nakwera Hezekiya kumka ku nyumba ya Yehova, namfunyulula pamaso pa Yehova.

15. Napemphera Hezekiya pamaso pa Yehova, nati, Yehova Mulungu wa Israyeli wakukhala pakati pa akerubi, Inu ndinu Mulungu mwini wace, Inu nokha, wa maufumu onse a dziko lapansi; munalenga kumwamba ndi dziko lapansi.

16. Cherani khutu lanu, Yehova, nimumve; tsegulani maso anu, Yehova, nimupenye; ndipo imvani mau a Sanakeribu, amene anatumiza kutonza nao Mulungu wamoyo.

17. Zoona, Yehova, mafumu a Asuri anapasula amitundu ndi maiko ao,

18. naponya milungu yao kumoto; popeza sindiyo milungu koma yopanga anthu ndi manja ao, mtengo ndi mwala; cifukwa cace anaiononga.

Werengani mutu wathunthu 2 Mafumu 19