1. Ndipo kunali, atamva Hezekiya, anang'amba zobvala zace, napfundira ciguduli, nalowa m'nyumba ya Yehova.
2. Natuma Eliyakimu woyang'anira nyumbayo, ndi Sebina mlembi, ndi akuru a ansembe opfundira ciguduli, kwa Yesaya mneneri mwana wa Amozi.
3. Nati kwa iye, Atero Hezekiya, Lero line ndilo tsiku la cisautso, ndi la kudzudzula, ndi la kunyoza; pakuti ana anafikira kubadwa, koma palibe mphamvu yakubala.
4. Kapena Yehova Mulungu wanu adzamva mau onse a kazembeyo, amene anamtuma mfumu ya Asuri mbuye wace, kuti atonze Mulungu wamoyo, nadzamlanga cifukwa ca mau adawamva Yehova Mulungu wanu; cifukwa cace uwakwezere otsalawo pemphero.