Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

2 Mafumu 19:1-3 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

1. Ndipo kunali, atamva Hezekiya, anang'amba zobvala zace, napfundira ciguduli, nalowa m'nyumba ya Yehova.

2. Natuma Eliyakimu woyang'anira nyumbayo, ndi Sebina mlembi, ndi akuru a ansembe opfundira ciguduli, kwa Yesaya mneneri mwana wa Amozi.

3. Nati kwa iye, Atero Hezekiya, Lero line ndilo tsiku la cisautso, ndi la kudzudzula, ndi la kunyoza; pakuti ana anafikira kubadwa, koma palibe mphamvu yakubala.

Werengani mutu wathunthu 2 Mafumu 19